Mwambo waukulu wokondwelera kubadwa kwa Radio Maria Malawi akuti udzachitika pa 2 september 2017 ndi mphwando la mayimbidwe (Radio Maria Malawi Choir Festival 2017) ku likulu la wailesi-yi ku Mangochi.
Malingana ndi malipoti a mu komiti yomwe ikuyendetsa dongosolo la mwambo-wu ati mphwando la mayimbidwe mu kwaya festival ya Radio Maria ya chaka chino , lidzakachitikira ku St Augastine Parish ku Mangochi Cathedral pa 2 september 2017.
Padakalipano makwaya ochokera mmadayosizi osiyanasiyana mdziko muno alembetsa kale ndipo ati azafika ndi kudzatenga nawo mbari pa tsikuli. Radio Maria Malawi inabadwa pa 24 August 2017 ndipo kufikira pano yakwanitsa zak 18 ikufalitsa uthenga wachipulumutso pa dziko lonse.