Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Bambo Chingale Asankhidwa Kukhala A Vicar Genenal A Dayosizi Ya Mangochi.

$
0
0

Episikopi wa mpingo wakatolika mu dayosizi ya Mangochi olemekezeka Ambuye Montfort Stima wasankha bambo Frank Chingale kukhala Vicar General wa dayosizi-yi kuyambira pa 30 August 2017.

Padakalipano mkulu wa kuofesi ya zofalitsa nkhani ndi mauthenga osiyanasiyana mu dayosiziyo bambo Emmanuel Malipa  afunira zabwino bambo-wa pomwe akhale akutumikira mpingo pa udindo-wu.

Iwo ati bambowa ngakhale asankhidwa kukhala nduna ya a episikopi a dayosizi akhala akupitilizabe kutumikira mpingowu ngati mkulu wa kuofesi yoona za maphunziro mu dayosiziyo.

Bambo Chingale asankhidwa pa undinowu polowa m’malo mwa malemu bambo Andrew Nkhata omwe anali Vilcar General a dayosiziyi


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>