Zotsatira za mayeso a Junior Certificate omwe ophunzira a form 2 analemba m’dziko muno akuti zatuluka.
Bungwe la New Independent Academic Examination Council ndi lomwe linagwira ntchito yolembetsa mayeso-wa.
Polankhula kwa atolankhani mu m’dzinda wa Blantyre mkulu wa bungwe-li mayi Phyles Kachingwe ati zotsatilazo zaonetsa kuti ophunzira ambiri omwe analemba nawo mayeso-wa sanachite bwino.
Iwo ati kuthetsedwa kwa mayeso-wa ndi boma ndi zina mwa zimene akuziganizira kuti ndi zomwe zakhala zikukolezelanso kusachita bwino kwa ana pa maphunziro awo.