Episikopi wa mpingo wakatolika mu dayosizi ya Zomba olemekezeka Ambuye George Desmond Tambala alimbikitsa ansembe mu dayosiziyo kuti apitirilize kuthandiza Radio Maria Malawi.
Ambuye Tambala anena izi pa msonkhano wa ansembe mu dayosiziyo, Iwo ati Radio Maria Malawi ndi wailesiyi imene ikudzipeleka pofalitsa uthenga wabwino kotero ansembe akuyenera kumalumikizana nayo ndi kuithandiza mu njira zosiyanasiyana.
Pamenepa ambuye-wa ati amsembe akuyeneranso kumagwilitsa ntchito wailesiyi pofalitsa mauthenga osiyanasiyana monga ma ulaliki komanso pochita ma pologalamu osiyanasiyana.