Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Apempha Akhristu Kudzipereka Pofalitsa Uthenga Wa Mulungu

$
0
0

Kudzipereka pa ntchito yakufalitsa uthenga wa Mulungu akuti ndi njira yokhayo  imene imaonetsa chikhristu chenicheni.

Abusa Joseph Maganga a mpingo wa CCAP  kuchokera ku Chiradzulu ndi omwe anena izi pofotokozera mtolankhani wathu. Iwo anati njira zofalitsira uthenga wa Mulungu ndi zambiri, ndipo ina mwa iyo ndi mawailesi a mipingo omwe tili nawo mdziko muno. Pamenepa m’busa Maganga wapempha akhristu kuti adzikonda kuthandiza Radio Maria yomwe nthawi zonse imakangalika kufalitsa uthenga wa Mulungu

Mwa zina m’busa Joseph Maganga pamodzi ndi akhristu ena kuchokera ku mpingo wa CCAP  anayamikira maprogramu amene wailesiyi imaulutsa ponena kuti ndiwothandiza zedi. 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>