Ofesi yoona za kalembera m’boma la Zomba yati anthu amene sanalembetse mayina awo mkaundula wa ziphatso za umzika asadere nkhawa kamba koti ofesiyi ikupitilizabe kulemba anthu ku maofesi a bwana mkubwa wa bomalo.
Wachiwiri kwa mkulu wowona zakalembala-yu m’bomalo a mayi Mercy Satumba ndi omwe anena izi pofotokozera mtolankhani wathu.
Iwo ati bomalo likufunitsitsa kuti ali yense alembetse ndi kukhala ndi chiphatso cha umzika.