Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Mmodzi mwa Oyang’anira Chisankho Mdziko la Kenya Atula Pansi Udindo

$
0
0

Mmodzi mwa akuluakulu a bungwe loyendetsa chisankho mdziko la Kenya la Independent Electoral and Boundaries Commission (IEBC) watula pansi udindo wake patangotsala masiku ochepa kuti dzikolo lichititse chisankho cha chibwereza cha pulezidenti.

Malinga ndi malipoti a wailesi ya BBC, mayi Roselyn Akombe wati watula pansi udindo wake kaamba koti bungwe loyendetsa chisankholo likugwira ntchito pansi pa ndale ndipo likulephera kupanga ziganizo zomveka bwino pa lokha.

Mayiyu amene padakali pano ali mdziko la America wati wachoka mdzikolo pofuna kuteteza moyo wake kaamba koti wakhala akulandira mauthenga omuopseza.

Sabata yatha mtsogoleri wa zipani zotsutsa boma dzikolo a Raila Odinga analengeza kuti sapikisana nawonso pa chisankho cha chibwerezachi chomwe chikuyembekezeka kuchitika pa 26 mwezi uno.

Bwalo lalikulu la milandu la dzikolo linayimitsa kaye zotsatira za chisankho cha pulezidenti chomwe chinachitika mdzikolo pa 18 August chomwe chinapeza kuti mtsogoleri wa dzikolo a Uhuru Kenyatta ndi omwe anapambana ati kaamba koti panali zina zomwe sizinayende bwino.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>