Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

AKHRISTU 23 APITA KU MALO OYERA KU ROME MWEZI WA MAWA

$
0
0

Akulu akulu omwe akuyendetsa zokonzekela za ulendo wa akhristu a ku Malawi opita kumalo oyera ku Rome mdziko la Italy pa 16 April chaka chino ati zokonzekera za ulendowo zili mkati ndipo zikuyenda bwino.

Polankhula lachinayi ku Maula Cathedral mu arch diocese ya Lilongwe pambuyo  pokumana ndi akhristu omwe ali pa ulendowu Bambo Joseph Kimu omwe ndi mkulu wa mapulogalamu ku Radio Maria Malawi anati ulendowu ungakhale opambana ngati akhristuwa angazindikile koposa zaulendowu.

‘’Timasankhana maudindo ena ndi ena monga wapampando, mlembi, oyang’anira zakudya, azofalitsa nkhani, achipembezo, owona zachipatala ndi zina zotero. Ngakhale tilipo anthu 23 amene tikupita ku Rome tinaona kuti mchoyenera kuti gulu limeneli likhale ndithu lokonzekera bwino kuti aliyense azikachita zimene akuzidziwa.’’ Anatero Bambo Kimu.

Malinga ndi Bambo Kimu pa ulendowu akhristuwo akapemphera ku malo osiyanasiyana oyera.

‘’Ukoko kukakhala kuwona malo osiyanasiyana koma chachikulu chomwe titi tikakondwere  kuchita ndi pa 27 April pamene Papa azalengeze kuti Papa Yohane 23 ndi woyera komanso Papa Yohane Paulo wachiri ndi oyera. Pa 28 April madzulo tizikanyamuka kubwerera kuno ku Malawi ndipo pa 29 ndi kumafika kunoko.’’ Anatero Bambo Kimu

Bambo Kimu anati ulendowu ndi wachinayi omwe akhristu akuno ku Malawi akhala akupita kunja ku malo osiyanasiyana oyera ndipo anati anthu ambiri omwe anapita mmaulendo amtunduwu akupereka  umboni za madalitso ochuluka omwe akumalandira chifukwa cha maulendowa.    

“Ulendo woyamba oyera ndinakonza mchaka cha 2000 pamene timakondwerera Jubilee ya zaka 2000 chibadwire Ambuye Yesu ndipo tinatenga anthu 62. Ulendo wachiwiri ndinakonza mchaka cha 2011, ndinatenga anthu 52 kupita ku Yerusalemu ndipo ulendo wachitatu mchaka cha 2012 ndinatenga anthu 47 kupita nawonso ku  Yerusalemu. Tsopano uwu ndi ulendo wachinayi umene ndikuwatenganso anthu kupita ku Rome ndipo mwina chaka chamawa tizawatenganso anthu kupita ku Yerusalemu.” Anatsiriza motero Bambo Kimu.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>