Anthu oyendetsa galimoto mdziko muno ati ali ndi udindo wopititsa patsogolo chitukuko cha dziko lino.
Wapampando wa bungwe la ma dalaivala mdziko muno la Drivers Association of Malawi, a John Harrison Banda anena izi ku Balaka pa mwambo wokhazikitsa bungweli m’bomalo.
Iwo ati madalaivala akuyenera agwire ntchito modzipereka kaamba koti kupanda iwo ntchito zambiri sizingayende bwino mdziko muno.
A Banda apempha madalaivala kuti agwirane manja pochepetsa ngozi za pansewu zomwe zikuchulukira mdziko muno.