Mpingo wa CCAP mu Sinodi ya Blantyre wachita mapemphero apadera, opempha mulungu, kuti adalitse dziko lino ndikulipatsa mvula yabwino.
M’modzi mwa akulu-akulu mu mpingo-wu, m’busa Alex Maulana, wati mpingo wa CCAP mu Sinodi-yi wachita mwambowu kaamba kokhudzidwa ndi malipoti akusowa kwa mvula m’madera ochuluka m’dziko muno.
Iwo ati ngati zinthu zitapitilira kukhala chomwechi ndiye kuti dziko lino litha kukomananso ndi mavuto a njala zomwe zingasokoneze miyoyo ya anthu mdziko muno.
Iwo ati akukhulupilira kuti mapephero omwe mpingowu wachita abala zipatso zabwino komanso kuti mulungu ayankha mapempherowa.