Mabungwe omwe si aboma ati akugwilizana ndi njira yoti aliyense akalembetse simu-kadi yake ya foni kamba koti zimenezi ndi zothandiza pa chitetedzo cha onse omwe amagwilira ntchito njirayi polumikizana ndi ena mosavuta.
AUndule Mwakasungula, ndi omwe anena izi m’boma la Mangochi, polankhula ndi mtolankhani wathu utangotha msonkhano wa mthumwi zoyimira mabungwe-wa ndi bungwe la Malawi Communication Regulatory Authority (MACRA) lomwe lakhadzikitsa ntchito yakalembera wa ma sim-kadi-yidziko muno.
Polankhulanso m’modzi mwa akulu-akulu ku bungwe la MACRAmayi Clara Mwafulirwa watsimikizira anthu m’dziko muno kuti asanyozere koma kukalembetsa ma simu- kadi awo mmasiku omwe akhadzikitsidwawa.
Ntchito yolembetsa masim-card a foni yomwe bungwe laMACRAlakhadzikitsa ikuyembekezeka kufika ku mapeto pa 31Marchchaka chino.