Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Bwanamkubwa wa Balaka Apempha Mgwirizano

$
0
0

Khonsolo ya boma la Balaka yapempha kuti pakhale ubale wabwino pakati pa adindo ndi makomiti a za chitukuko m’bomalo.

Bwanamkubwa wa bomalo, Rodrick Mateauma ndi yemwe wanena izi potsatira mphekesera yomwe yakhala ikumveka yoti  magulu awiriwa sakulumikizana pa ntchito  zachitukuko m’bomalo.

Iye watinso zikuonetsa kuti vuto lonseli likuchitika kaamba koti makhansala ena sakuzindikirabe udindo wawo ndi zoyenera kuchita izi ndi zimene zikuchitisa kuti makomiti achitukuko ndi makhansalawa adzisemphana pakagwiridwe ka ntchito.

Polankhulapo  m’modzi mwa makhansala a m’bomalo Peterson Bwanali  wathirirapo ndemanga  kuti  ubale wa magulu awiriwa wakhala usakuyenda bwino m’bomalo.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>