Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Chisankho Chapadera Cha Pulezidenti Mdziko la Zambia Chichitika Mwezi wa January

$
0
0

Chisankho cha pulezidenti chapadera mdziko la Zambia chichitika pa 20 January chaka cha mawa pofuna kupeza mtsogoleri yemwe alowe mmalo mwa mtsogoleri wakale wa dzikolo malemu Micheal Sata.

Mtsogoleri wogwirizira Guy Scott, yemwe malamulo adzikolo sakulola kuti adzapikisane nawo paudindowu, kamba koti makolo ake sanali nzika za dzikolo.

Iye walengeza izi lachiwiri ndipo wapempha atsogoleri a ndale mdzikolo kuti asunge bata ndi mtendere.

Padakali pano  mchipani cholamula cha Patriotic Front muli kusamvana kamba koti  Pulezidenti Scott anachotsa mlembi wamkulu wachipanicho pa 3 November popanda chifukwa chenicheni.

Pulezidenti wa dzikolo Michael Sata anamwalira lachiwiri pa 28 October pa chipatala cha King Edward 7 mumzinda wa London ndipo anaikidwa mmanda lachiwiri pa 11 mwezi  uno.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>