Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Bungwe la CADECOM Lilimbikitsa Alimi Kukhala Odzidalira

$
0
0

Bungwe lowona za chitukuko mumpingo wa katolika la Catholic Development Commission in Malawi (CADECOM)  m`boma la  Dedza lakhazikitsa ntchito ya zaka zitatu yotchedwa Zuze Intergrated Food Security pofuna kuthandiza alimi osauka kukhala odzidalira pachuma.

Mkulu wabungweli mudayosiziyo a Patrick Namakhoma ati ntchito imeneyi ithandiza kuchepetsa mavuto a chakudya kwa mabanja amene ali osowa kuti mabanjawa azipeza ndalama mosavuta.

Iwo ati cholinga cha ntchitoyo  ndi kulimbikitsa ulimi wa mbewu komanso wa ziweto ngakhalenso  ma banki a ku mudzi ndi cholinga chakuti anthu azitha kupanga ma bizinesi ang’onoang’ono.

Mwa zina,bungweli likhalanso likulimbikitsa ntchito yopereka madzi abwino komanso mbewu zamakono kwa alimiwa.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>