Chipani cholamula mdziko la Zambia cha Patriotic Front chayimika Pulezidenti wadzikolo Guy Scott kukhala membala wachipanicho kwa miyezi iwiri.
Chipanicho chayimika Pulezidenti Scott yemwe akugwirizira udindowu kamba kochita zinthu mosatsata malamulo.
Zinthu sizikuyenda bwino kwenikweni mchipanicho pamene anthu akuyembekezeka kusankha mtsogoleri yemwe alowe mmalo mwa Pulezidenti Michael Sata, yemwe anamwalira pa 28 October chaka chino ali pa udindowu.
China mwa Zifukwa chomwe Pulezidenti Scott akudzudzulidwa nacho ndi kukakamiza atolankhani maka a nyumba zofalitsa nkhani za boma kulemba nkhani zabwino zokhudza iye yekha.
Chisankho chapadera mdzikolo chichitika pa 20 January chaka cha mawa ndipo Pulezidenti Scott sadzayima nawo kamba koti si nzika ya dzikolo.