Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

A ku Banja Adzudzula Madonna Polephera Kusunga Lonjezo

$
0
0

Katswiri woyimba nyimbo za chamba cha POP wa mdziko la America Madonna, amudzudzula kamba kolephera kusunga lonjezo lomwe anapereka kwa makolo a mwana yemwe anamutenga mdziko muno kuti akamulere mdziko la kwawo.

Mayi Lucy Chekejiwa omwe ndi gogo wa Mercy James mmodzi mwa ana omwe iye adawatenga ndi omwe anena izi pofotokozera Radio Maria Malawi mu mzinda wa Blantyre.

Gogo Chekejiwa ati zaka zisanu ndi ziwiri zadutsa kuchokera pomwe Madonna anatenga mwanayo  koma mpaka pano, aku banja sadamuonepo.

Iwo ati ndi zodandaulitsa kuti Madonna amafika mdziko muno koma safuna kuwadziwitsa a ku banja  kuti mwanayo wafika mdziko muno.

“Ndakhala ndikudikira kuti mwina mwana abwera ndidzacheze naye, koma chimutengere sanayambe wabwerapo, mwanayo ndi wathu tikufuna titamuona,” anatero mayi Chekejiwa.

Iwo ati achita izi kamba kopwetekedwa mtima poganizira nthawi yomwe yadutsa asadamuone mdzukulu wawo ndipo apempha onse omwe angathe kuti alowelerepo pofuna kupeza mwayi womuona mwana wawo.

Madonna anatenga ana awiri a masiye mdziko muno David Banda ndi Mercy James kuti akawalere mdziko lakwawo ndipo pulezidenti wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika sabata yatha wasankha katswiri woyimbayu kuti akhale kazembe pa kasamalidwe ka ana.

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>