Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Radio Maria Iyamikira Akhristu a ku Mangochi Cathedral

$
0
0

Akhristu a mu Parish ya St.Augustine Mangochi Cathedral mu dayosizi ya Mangochi awayamikira chifukwa  chothandiza Radio Maria Malawi.

Mkulu woona za chithandizo ku wailesiyi Mayi Veronica Manyozo ndi omwe ayamikira akhristuwa pa mwambo wa nsembe ya misa ya promotion womwe unachitika ku parish yi lamulungu pa 14 December.

Iwo alimbikitsa abwenzi a wayilesiyi  komanso akhristu  kuti asatope ndi ntchito yayikulu yomwe akugwira pothandiza kupeza thandizo loyendetsera wailesiyi.

Bambo mthandizi wa Parish yi Bambo Fanuwel Masakatila anathokoza akhristuwa kamba ka chidwi chomwe ali nacho chothandiza wailesiyi ndipo  awambikitsa kuti apitilize kuyithandiza  mu njira zosiyanasiyana zimene angakwanitse.

Pa mwambowu anthu anathandiza Radio Maria Malawi ndi ndalama zopitilira 2 hundred thousand kwacha.

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>