Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Zokonzekera Mwambo wa Chikondwelero cha Kachebere Seminale Zikuyenda Bwino

$
0
0

Zokonzekera  mwambo otsekulira chikondwelero chakuti  sukulu yosulira ansembe ya Kachebere m’boma la Mchinji yatha zaka 75 chiyambire ntchito zake akuti zikuyenda bwino.

Wapampando wa komiti yomwe ikuyendetsa ntchito zokonzekera chikondwelerochi Bambo George Nyanga ndi omwe anena izi lachitatu polankhula ndi Radio Maria Malawi.

Bambo Nyanga ati mwambo otsekulira chikondwelerochi, uchitika loweruka pa 10 mwezi uno,ndipo pa 10 October 2015 ndipamene chikondwelerochi chizachitike.

Iwo ati zokonzekera za chikondwelerochi zikuyenda bwino kamba koti akhazikitsa ma komiti osiyanasiyana omwe  akugwira ntchito yokonzekera mwambowu.

Mwambo otsekulira chikondwelerochi loweruka likudzali, udzayamba ndi  nsembe ya misa yomwe ikuyembekezeka kudzatsogoleredwa ndi Episkopi wa Dayosizi ya Karonga Ambuye Martin Mtumbuka,omwenso ndi wapampando oyang’anira ntchito  msukulu zosulira ansembe mdziko muno.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>