Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Mchitidwe Wozembetsa Anthu Akuti Ukupitilirabe M`boma la Mangochi

$
0
0

Bungwe la Rights Advice Center m’boma la Mangochi lati lakonza mapulani omwe athandize kuthana ndi m’chitidwe wozembetsa anthu m’bomalo.

Mkulu wa bungweli m’bomalo a Madalitso Masache ndi yemwe wanena izi pofotokozera mtolankhani wathu , yemwe  amafuna kudziwa ntchito zomwe bungweli lakonza kuti ligwire  m’chakachi.

Iwo ati  bungwe lawo litachita kafukufuku, lapeza kuti mchitidwe wozembetsa anthu ukupitilira  m’boma la Mangochi.

“Tagwirizana ndi bungwe la Ma Judge komanso ma Magistrate kuti asule  anzathu apolisi komanso a Immigration maka amene amakhala malire adziko pa nkhani zozembetsa anthu, komanso tikhala ndi maphunziro mmadera osiyanasiya owaziwitsa anthu kuyipa kwa mtchitidwe ozembetsa anthu”, anatero a Masache.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>