Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Madzi Apha Munthu M`modzi Ndikuvulaza ena Atatu M`boma la Zomba.

$
0
0

Munthu m’modzi wafa ndipo ena atatu akuti  avulala ndi madzi osefukira mu m’tsinje wa Likangala  m’boma la Zomba.

Malinga ndi Wofalitsa nkhani za apolisi m`boma la Zomba  Constable Patricio Supliano ati, madzi a mphamvu ochokera ku mtunda kwa mtsinjewu anabwera ochuluka  ndipo munthu mmodzi ndi yemwe wamwalira atakokololedwa ndi madziwa ali mnyumba mwake, ndipo ana ena atatu avulala kwambiri chifukwa cha madziwo, ndipo akulandira chithandizo pa chipatala chachikulu cha Zomba.

Madziwa awononga kwambiri nyumba komanso katundu wosiyanasiyana.Mtsinje wa Likangala ku Zomba wadutsa midzi ya  Sadzi, Namalaka komanso MPondabwino.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>