Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Papa Francisco Wayamikira Akhristu aku Japan Chifukwa cha Chikhulupiliro Cholimba

$
0
0

Mtsogoleri wampingo wakatolika padziko lonse Papa Francisco,wayamikira akhristu a mpingowu mdziko la Japan chifukwa cholimba pa chikhulupiliro chawo,ngakhale akhala akukumana ndi mavuto osiyanasiyana kuphatikizapo achilengedwe.

Papa Francisco,amalankhula izi lachisanu pa mkumano omwe anali nawo ndi maepiskopi a mdziko la Japan-lo omwe ali paulendo okacheza kulikulu la mpingowu  omwe maepiskopi mumpingowu padziko lonse amakhala nawo pakatha zaka zisanu.

Iye wawuza ma episkopiwo, kuti kulimba mtima pachikhulupiliro komwe akhristu a mdzikolo akhala akuwonetsa,ndi phunziro lalikulu kwa akhristu onse mumpingowu kuti asamafowoke pa chikhulupiliro chawo.

Mtsogoleri wampingo wakatolikayu anatchulapo ngozi ya tsunami, nkhondo yomwe idawononga dzikolo zaka makumi asanu ndi awiri zapitazo komanso kupezeka kwawo pakati pa anthu osakhulupilira Mulungu, kuti ndi zina mwa zovuta zomwe iwo akhala akupilira.

Iye wayamikiranso maepiskopiwo chifukwa cha ntchito yayikulu yomwe akhala akugwira potukula maphunziro, umoyo komanso za chifundo kwa anthu osowa ndi zina zambiri.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>