Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Ma Episkopi Makumi Anayi ndi omwe Akakhale Nawo pa Msonkhano Wachiwiri Wokhudza Banja

$
0
0

Mtsogoleri wampingo wakatolika padziko lonse Papa Francisco, wavomereza mayina a maepiskopi a mmayiko  makumi anayi omwe mabungwe a maepisikopi mmayikowa asankha kuti akawayimilire pa msonkhano wachiwiri  wa maepiskopi okambirana nkhani zokhudza banja.

Papa Francisco wavomereza nthumwizi kumsonkhanowu, pambuyo povomereza zina zochokera mmayiko makumi atatu mmwezi wa January.

Msonkhanowu, ukuyembekezeka kudzachitikira kulikululo m’mwezi October chaka chino.

Zina mwa nthumwi zomwe zikuyembekezeka kudzakhala nawo pa msonkhanowo zomwe Papa Francisco wazivomereza posachedwapa ndi Cardinal Reinhard Marx, Cardinal Jorge Urosa Savino wa mdziko la Caracas komanso Arkbishopu Philip Tartaglia waku Glasgow ku England.

 

 

 

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>