Quantcast
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Unduna wa Zaumoyo Walimbikitsa Anthu kuti Apewe Matenda a Makutu

Unduna wa zaumoyo walangiza  anthu mdziko muno kuti apewe mchitidwe omvera zinthu zomwe zikupereka phokoso lopitilira muyeso pofuna kupewa matenda a khutu.

Nduna ya za umoyo Dr. Jean Kalirani ndi yomwe yapereka langizoli Lachisanu pa chipatala cha Queen Elizabeth Central mu mzinda wa Blantyre pamwambo wokumbukira kufunika kwa makutu.

Dr Kalirani ati anthu ambiri amakonda kutsekula zoyimba mopitilira muyeso, kumvera nyimbo pogwiritsa ntchito zipangizo zamakono zomvera paulendo ndi zina zambiri zomwe zikukolezera matenda a khutu.

‘Mavuto ena a kusamva amabwera chifukwa chokonda kumvera zinthu zokwezedwa kwambiri zomwe nthawi zina zimadzetsa mavuto a makutu,’anatero a Kalirani.

Iwo alimbikitsa anthu kuti  akaona kuti mkhutu mwawo muli vuto asamazengereze koma azithamangira ku chipatala.

Pothilirapo ndemanga dotolo wowona za matenda a khutu pa chipatalacho  Dr Wakisa Mulwafu, wati mdziko muno muli anthu pafupifupi 650 sauzande omwe amavutika ndi nthendayi  zomwe zikutanthauza kuti vutoli ndi lalikulu kwambiri.

Padakali pano boma linakhazikitsa chipatala chapadera ku chipatala chachikuluchi ndi cholinga choti anthu amene amavutika ndi nthendayi azithandizika.

 

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>