Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

A Mipingo Atengepo Gawo Lolimbana ndi Matenda a Edzi

$
0
0

Bungwe la atolankhani lolimbana ndi matenda a Edzi la Journalist Against Aids, lati matendawa  m’dziko muno angachepe ngati a mipingo atadzipereka pofalitsa kuopsa kwa matendawa akakhala m’makachisi awo.

Mkulu wa bungweli  a Christopher Bauti, ndi yemwe wanena izi Lachisanu mu mzinda wa Lilongwe, pa mkumano watsiku limodzi wa bungweli ndi  akuluakulu a mipingo yosiyanasiyana.

A Bauti ati amipingo angatengepo mbali yayikulu pa ntchito yofalitsa uthenga wokhudza kuwopsa kwa matendawa kudzera mu magulu osiyanasiyana omwe akhristu amakumana.

‘Tinaona kuti mbali imodzi yofalitsira ma uthenga a matendawa ndi kudzera mwa  akuluakulu a mipingo kamba koti munthu aliyense amakhala ndi nthawi yopita kukapembedza,’ anatero a Bauti.

Iwo ati ndi wokondwa kuti mmipingomo muli magulu osiyanasiyana zomwe zithandize mu kafalitsidwe ka ma uthengawa.

Bungweli lakhala likugwira ntchitoyi ndi mabungwe, akuluakulu a ndale ngakhalenso boma la dziko lino pofuna kuwonetsetsa kuti chiwerengero cha matendawa chikuchepa.

 

 

 

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>