Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Mwana wina Watenthedwa chifukwa cha Chikhristu

$
0
0

Mwana wina wa chipembedzo cha chikhristu mdziko la Pakistan waphedwa potenthedwa  ndi moto wa mafuta a Petulo atapezeka akuwuza anthu kuti iye ndi mkhristu.

Malipoti ati mwanayu Noman Masih, anali wa zaka khumi ndi zitatu zakubadwa ndipo wakhala akunena izi mosabisa  zomwenso anthu ena amakwiya nazo.

Anthu awiri omwe sakudziwika,ndi omwe apha mwanayo.

Padakalipano, mkulu wa bungwe lomenyera ufulu wa akhristu m’dzikomo  Mervyn Thomas, wati bungweli  ndi lokhudzidwa kwambiri  ndi imfa ya mwanayo.

Iye wapempha boma la dzikolo kuti lithandize kupereka chitetezo chokwanira kwa akhristu amene akuzunzidwa munjira zosiyanasiyana ndi anthu odana ndi chipembedzochi.

Dziko la Pakistan ndi lili ndi chiwerengero chachikulu cha anthu otsatira chipembedzo cha chisilamu.

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>