Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Asilikali a Mdziko la Nigeria Apulumutsa Amayi ndi Ana ku Zigawenga za Boko Haram

$
0
0

Dziko la Nigeria likusunga amayi ndi ana omwe apulumutsidwa mmanja mwa zigawenga za Boko Haram ku malo ena a asilikali pofuna kuti liziwasamalira mwanjira zosiyanasiyana.

Kumalo a asilikaliwo,amayiwo azilandira uphungu pankhani zosiyanasiyana ndi cholinga choti ayiwale nkhanza zomwe akhala akukumana nazo.

Dzikolo latinso lili ndi nkhawa pomwe likukayikira kuti ena mwa amayiwo atha kukhala ataphunzira moyo wankhanza kwa zigawengazo.

Malipoti ati panthawi yomwe amayiwo amasungidwa mmisasa ya boma amai ena amawonetsa zizindikiro zoti akumalumikizana ndi mamembala a mgulu la zigawengalo


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>