Zokonzekera chikondwerero choti Dayosisi ya Chikwawa yatha zaka 50 chiyikhazikitsileni mdziko muno akuti ikuyendabwino.
Ambuye Musikuwa amu Dayosisiyi anena izi poyankhula ndi Radio Maria ndipo anati ngati Dayosizi, yakhazikitsa magulu osiyanasiyana omwe akuyendetsa dongosolo la chaka cha chikondwererochi chomwe chidzachitike pa 29 August chaka chino.
“Dayosisi ili pakalikiliki yokangagalika kukodzekera mwambo wa Golden Jubilee ndipo pali zithu zingapo zomwe takonza kuti tichite. Choyamba kukonza Golden Jubilee Celebration Committee, chachiwiri kuwona mmene mpingo wagwilira ntchito yake kuno ku Dayosisi ya Chikwawa pa dzaka 50.”anatero a Bishop Musikuwa.
Iwo anapitiliza ponena kuti akuyenela kuchita izi ndicholinga choti akonzekere mmene angathe kuyendetsera ntchito ya mpingo pazaka 50 zikubwelazi.
“ mwambo udzafika pachimake penipeni pamene tidzankhala tikuchita mwambo wa nsembe yamisa pa 29 August chaka chomwe chino ndipo nkati mwachikodwelerochi muli zambiri zochitika.”antero Ambuye Musikuwa.
Dayosiziyi alindi mapulani wokhala ndi wailesi yawoyawo, kumanga malo a achinyamata komanso kumanga tchalichi chachikulu chatsopano komanso kuwonjezera magulu a chipembezo,zomwe zikhazikitsidwe posachedwa.