Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Radio Maria Malawi Iyamikira Akhristu Pothandiza pa Mariatona

$
0
0

President wa Radio Maria Malawi a Nicholus Chonde wayamikira akhristu omwe akhala akuchitapo kanthu pothandiza Radio Maria Malawi m’masiku a Mariatona kuyambira pa 15 May mpaka pa 27 June 2015 yomwe imachitika ndi cholinga chofuna kupeza thandizo la  ndalama zoposera 15 Million Kwacha zothandizira ntchito yomangira Transmitter m’boma la Thyolo. .

A Chonde amalankhula izi loweruka pa mwambo wotsekera International Mariatona-yu ku phiri la Michiru  ku Chilomoni mu Arch diocese ya Blantyre.

Iwo ati ali ndi chikhulupiliro kuti thandizo lomwe akhristu achita lithandiza  wailesiyi  kukwaniritsa zolinga zake.

Polankhula wapampando wa abwenzi a Radio Maria Malawi mu Archdiocese-yi a Joseph Rappozo ati abwenzi a wailesiyi mu Archdiocese-yo apitiriza kudzipereka pothandiza wailesiyi kuti ikwaniritse zolinga zake

M’mawu ake mkulu woona ntchito za ma pologalamu ku wailesiyi Bambo Joseph Kimu alimbikitsa abwenzi a wailesiyi mdziko muno kuti azionetsanso chidwi potenga nawo mbali yokonza komanso kuwulutsa  ma pologalamu osiyanasiyana pogwiritsa ntchito luso ndi mphatso zomwe ali nazo.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>