Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Ulendo wa Papa Francisco Mdziko la USA Udzakhala Wopindula

$
0
0

Maepiskopi a mpingo wa katolika mdziko la United States ati akuyembekezera kuti ulendo wa Papa Francisco mdzikolo womwe uchitike mmwezi wa September  udzakhala wopindula.

 

Malipoti a Catholic News Agency ati pa ulendo wa masiku asanu ndi anayiwa pambuyo poyendera dziko la  Cuba komwe akakumane ndi atsogoleri a zipani zosiyanasiyana, Papa Francisco adzakayenderanso madera ena atatu mdziko la United States. 

Maepiskopi am’maderawa atamva izi anali okondwa kaamba koti anachiwona chinthu cha mtengo wapatali kuyenderedwa ndi mtsogoleriyu.

Papa Fransisco akatsirizira ulendo wakewu  pokumana ndi President wa dzikolo  Barrack Obama.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>