Kupereka mwayi ku mabungwe osiyanasiyana omwe siaboma kutenga nawo gawo pa ntchito zokhudza magetsi mdziko muno ati kungathandize kuti mitengo yamagetsiwa ikhale yotsikirapo.
Wofalitsa nkhani ku unduna wa zamigodi mphamvu zamagetsi zachilengedwe ndi nyama zakuthengo a Josephy Kalowekamondi womwe anena izi polankhula ndi Radio Maria Malawi pomwe imafuna kumva zambiri pa nkhani yofuna kugawa pawiri bungwe logulitsa magetsi mdziko muno la ESCOM kuti idzitha kukwaniritsa zofuna za anthu.
A Kalowekamoati anthu akuyenera kumvetsetsa kuti silikufuna kugulitsa bungwe la ESCOM koma kuti akufuna kuligawa kukhala nthambi ziwiri zomwe ndi yopanga magetsi komanso yogulitsa magetsi pofuna kukweza kagwiridwe ka ntchito ka bungweli.