Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Papa Benedict wa 16 ndi Wokhudzidwa ndi Mavuto omwe Anthu Othawa Kwawo Akukumana NawoPapa Benedict w

$
0
0

Mtsogoleri wampingo wakatolika wopuma Papa Benedict wa  16 ati ndi okhudzidwa ndi mavuto omwe anthu othawa kwawo chifukwa cha nkhondo komanso anthu omwe amachoka m`mayiko mwawo kamba kosowa ntchito, akukumana nawo.

Mlembi wa Papa Benedict  Arch bishop George Ganswein ndiye wanena izi atakhala nawo pamwambo wansembe ya ukaristia munzinda wa Ancona m`dziko la ITALY. 

Arch bishop-yu anati Papa wopumayu  ndi wokhudzidwa kwambiri kamba koti anthu ambiri akumataya miyoyo yawo pa nyanja  nthawi yomwe akuwoloka kupita tsidya lina ndipo ati Papa Benedicto akuwapempherela.

Pamwambo wansembe ya ukaristiyayi , anapemphereranso anthu onse omwe akumakakamizika kuchoka m`mayiko mwawo kamba ka nkhondo komanso mavuto osiyanasiyana.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>