Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Alimi Apewe Kugula Mbeu Wamba

$
0
0

Kampani yogulitsa  mbeu mdziko muno ya Mosanto Malawi yachenjeza alimi   kuti apewe kugula mbeu kwa mavendor.

Mkulu wa zamalonda ku kampaniyi a Denis Kachikho ndi omwe anena izi potsatira kumangidwa kwa a Mavuto Chilipa omwe apolisi   anawapeza akugulitsa mbeu yowonongeka    ya chimanga pa nsika wa Bvumbwe m’boma la Thyolo.

A Kachikho ati ma venda nthawi zina amapezeka ndi katundu wosayenera choncho ndi kofunika kuti alimi asamagule mbeu zawo.

Iwo apemphanso boma kuti liwunikenso malamulo ogulitsira mbeu ndi cholinga choti aliyense wopezeka akugulitsa mbeu yowonongeka azipatsidwa chilango chokhwima.

Pamenepa Iwo ati  mchitidwe wotere umabwezera m’mbuyo chitukuko ndinso njala m’dziko muno.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>