Anthu m’dziko la Sierra Leone akupitiliza kuchita chisangalalo chokondwelera kutha kwa matenda a Ebola m’dzikomo.
Bungwe la za umoyo pa dziko lonse la World Health Organization ndi lomwe lalengeza izi, potsatira kafukufuku yemwe lachita m’dzikomo.
Bungweli lati masiku 42 omwe linakhadzikitsa ofuna kufufuza ngati alipo munthu wina wodwala matenda atha zomwe zikupereka chitsimikizo chakuti matendawa atha m’dzikomo.
Matenda a Ebola anayamba m’dzikomo ndi mayiko ena oyandikana ndi dzikoli monga a Guinea, Liberia kuyambira mchaka cha 2013.
Malingana ndi malipoti anthu oposera 11 sausande ndi amene akuwaganizira kuti anafa atagwidwa ndi matendawa m’mayikowa.
Padakali pano ntchito yothana ndi matendawa ati ili mkati m’dziko la Guinea lomwe lachita malire ndi dzikolo.