Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Nsika wa Kasungu Ukufunika Ndalama Zokwana 10 miliyoni Kwacha

$
0
0

Nsika wa Kasungu omwe unapsa mwezi wa October ati ukufunika ndalama zoposa 10 Million Kwacha kuti ukozedwenso. 

Wachiwiri kwa Meya wa Manicipality ya Kasungu  a Ephate Joshua ndi yemwe wanena izi pomwe kampani yopanga cement ya  Shayona imapereka matumba a cement okwana 1 hundred 20 ku khonsoloyi ndi cholinga chothandizira ntchito yokonzanso  msikawu.

A Joshua ati motoyu unaononga zinthu zambiri kuphatikizapo maofesi ena  a khonsoloyi ndipo pafunika ndalama zokwana 10  million kwacha kuti zinthu zibwerelenso m`chimake.

Iwo ati padakali pano khonsoloyi ikulephera kutolera misokho mumsikawu zomwenso zikubwenzeretsa ntchito zake m`mbuyo.

M`mawu ake m`modzi mwa akuluakulu a kampani ya Shayona a Austin Mvula  anati apereka thandizoli kamba koti anamva za ngoziyi.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>