Akhristu a mpingo wa katolika a m’dziko la Central African Republic omwe akhala akuphana tsiku ndi tsiku kamba ka nkhondo ati akuyembekezera kuti ulendo wa mtsogoleri wa mpingo wa katolika pa dziko lonse Papa Francisco wokacheza mdzikolo m’mwezi uno uthandiza kuchepetsa mavuto omwe dzikolo likukumana nao.
Malinga ndi malipoti a News 24 ulendo wa Papa wokacheza mdzikolo upereka chiyembekezo kwa anthu a mdzikolo.
Anthu a mdziko la Central African Republic akhala akuphana kamba ka kusamvana kwa boma la dzikolo ndi magulu owukira.
Pa ulendowu Papa akuyembekezeka kukayendera malo omwe anthu akukumana ndi mavuto kamba ka nkhondoyi amakhala komanso mzikiti womwe umatchedwa kuti ndi woopsa mu mzinda wa Bangui ndipo pamapeto pake akachita mwambo wa nsembe ya misa pa bwalo lalikulu la masewero mdzikolo.
Papa akacheza mdzikoli pa 28 ndi pa 29 mwezi uno.