Bungwe la mpingo wa Akatolika la Community of St Egidio m’dziko muno layamba ntchito yophunzitsa anthu kufunika kwa kalembera wa ana omwe angobadwa kumene.
Polankhula pa mwambo otsegulira maphunziro a ntchitoyi omwe ukuchitikira mu mzinda wa Blantyre mkulu oyendetsa ntchito mu nthambi ya boma yoona za
kalembera ya National Registration Bureau a Francis Chinsinga ati ali ndi chikhulupiriro choti ntchitoyi iyenda bwino kamba ka m’gwirizano omwe ulipo pakati pa boma ndi bungweli m’dziko muno.
A Chinsinga ati ntchitoyi yomwe yayamba m’boma la Balaka ikuyembekezera kufalikira m’madera ena m’dziko muno.