Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Anthu Odwala Matenda a Edzi Asasalidwe

$
0
0

Bungwe  la National AIDS Commission NAC lati anthu omwe anapezeka ndi kachilombo koyambitsa  matenda a Edzi sayenera kusalidwa .

 

Mmodzi mwa akuluakulu ku bungweli  a Ahmidu Tung'ande ndi omwe anena izi mu mzinda wa Zomba pomwe amakumana ndi mabungwe a boma komanso omwe si a boma pomwe amawafotokozera momwe bungweli likugwilira ntchito zake.

A Tung'ande ati ndi cholinga cha bungweli kuti pomafika mchaka cha 2020 nthenda ya Edzi idzakhale itatha mdziko muno.

Iwo alangiza azipembezo zina mdziko muno kuti asiye mchitidwe woletsa akhristu awo omwe anapezeka ndi kachilombo ka HIV kuti asiye kumwa makhwala otalikitsa moyo a ARV kamba koti  munthu aliyense amene anapezeka ndi kachilomboka ali ndi ufulu womwa makhwalawa. 

 

A Tung'ande anatinso pali ana ena omwe anabadwa ndi kachilomboka ndipo apempha makolo amene ali ndi anawa kuti aziwonetsetsa kuti nthawi zonse akuwapatsa makhwala.

 

Mmau ake mkulu wa zaumoyo mu mzindawu a Gomezgani Nyasulu anati pakuyenera kukhala  mgwirizano wabwino pakati pa mabungwe omwe amagwira ntchito zokhudza matendawa m’bomalo.

 

Pomaliza a Nyasulu anayamikira bungwe la  NAC kamba ka ntchito yabwino yomwe likugwira yofuna kuthetsa matendawa mdziko muno.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>