Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Boma la Dziko la Egypt Alipempha kuti Lipereke Chitetezo ku Mipingo ya Mdzikolo

$
0
0

Mabungwe omenyala ufulu wa anthu mdziko la Egypt apempha boma la dzikolo kuti likhwimitse chitetezo ku mipingo ya  mdzikolo.

Ma bungwewa apereka pempheloli potsatira chiwopsezo chomwe mpingo wa Orthodox walandira kuchokera ku gulu la zauchifwamba la Jihadist.

Gululi ati likukonza zokachita zamtopola pa tchalitchi lina la mpingowu ndipo popereka chiwopsezocho lachita kufotokoza   malo omwe tchalitchilo limapezeka  komanso mmene chinamangidwira.

Padakali pano apolisi mdzikolo ati ayamba kale kuteteza malowo.

Gulu la Jihadist lakhala likupereka chiwopsezo ku magulu osiyanasiyana mdzikolo ndipo mu chaka cha 2011 gululi linachita zamtopola pa tchalitchi lina mdzikolo pomwe   anthu okwana 26 anaphedwa.    


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>