Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Bungwe la SA Medicines Control Council Livomela Mankhwala Othandiza kupewa Kachilombo ka HIV

$
0
0
Bungwe la South Africa Medicines Control Council mdziko la South Africa lavomeleza kuti mankhwala omwe anapangidwa pofuna kupewa kutenga kwa  kachilombo a HIV ayambe kugwira ntchito mdzikomo.

 

Mankhwalawa omwe akuwatchula dzina loti Truvada ndipo ndi ama pilisi akuyenera kumamwedwa tsiku lililonse .

Malipoti  a Nyuzi 24 ati  mankhwalawa athandizanso kuchepetsa chiwerengero    cha achinyamata omwe ndi apakati pazaka 15 komanso 20 kamba koti ndi gulu la anthu omwe ali pachiwopsezo chotenga kachilomboka.

Malinga ndi malipoti mankhwalawa cholinga chake chinali chofuna kuti azichiza   matenda a EDZI   koma atayesedwa, zotsatira  zapezeka kuti   zithandiza munthu amene alibe matendawa      kuti  asatenge   kachilomboka.

Mankhwala asanayambe kuperekedwa mzipatala za mdzikomo ati awona mmene angakhudzire ntchito ya zaumoyo mdzikomo. 

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>