Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Ana 1 Miliyoni a Mdziko la Nigeria ndi Mayiko Atatu Sakupita ku Sukulu

$
0
0

Malipoti a nthambi ya United Nations yoona za chisamaliro cha ana yapeza kuti chiwerengero cha ana 1 miliyoni a mdziko la Nigeria komanso maiko atatu oyandikana ndi dzikolo sakupita ku sukulu kaamba ka gulu la zigawenga za Boko Haram.

Malipoti a wailesi ya BBC ati sukulu zoposera 2 sauzande zinatsekedwa ndipo zina zinasandutsidwa malo okhalamo zigawengazo.

Pulezidenti wa dzikolo Muhammadu Buhari ati anauza asilikali a dzikolo kuti pomafika mapeto a mwezi uno, akhale atathana ndi zigawengazo ngakhale kufikira pano zigawengazo zikuponyabe mabomba mmadera osiyanasiyana mdzikolo.

Malinga ndi malipoti  kufikira pano zigawengazi zapha anthu okwana 17 sauzande ndipo anthu oposera 2 miliyoni akusowa pokhala.

Padakali pano gulu la zigawenga za Boko Haram linafalikira mmaiko a Cameroon, Chad komanso Niger omwe ndi oyandikana ndi dziko la Nigeria.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>