Anthu othawa kwao pafupifupi makumi anayi apezeka atafa pa nyanja ina boti lomwe anakwera litamira mdziko la Turkey.
Malipoti a nyuzi 24 ati ngoziyo yomwe ndi kuphatikizapo ana yachitika pomwe anthuwa amapita mdziko la Greece.
Ngoziyo ati yachitika kamba ka mphepo yamkutho yomwe inamenya pa nyanjayo.
Ngozi za mtunduwu zakhala zikuchitika kwambiri kwa anthu othawa kwawo kamba koti amafuna kukapeza mtendere mmayiko ena.