Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Munthu Mmodzi Wafa ndi Matenda a Ebola Mdziko la Liberia

$
0
0

Munthu m`modzi ati wafa  ndi matenda a Ebola m`dziko la Liberia patangotha miyezi yowerengeka, bungwe la zaumoyo pa dziko lonse litalengeza kuti nthendayi yatha m`dzikolo.

Malinga ndi malipoti awayilesi ya BBC, mzimayi yemwe ndi wa zaka 30 zakubadwa wamwalira pachipatala china mu mzinda wa Monrovia momwe muli anthu ochuluka.

Dziko la Guinea lomwe ndi loyandikana ndi dzikoli  mwapezeka anthu ochulukirapo omwe akudwala nthendayi.

Anthu oposa 11 sauzande  ochokera m`mayiko a Guinea , Liberia, komanso Sierra Leone  anafa ndi nthendayi mzaka ziwiri zapitazo.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>