Anthu m`dziko la Kenya achita mapemphero okumbukira mizimu ya anthu 148 omwe anafa pa chiwembu chomwe gulu la zigawenga za Al- Shabab zinachita pa sukulu ya ukachenjede ya Garisa m`dzikolo.
Malinga ndi malipoti awailesi ya BBC anthu mazanamazana anasokhana pa sukuluyo ndipo anachita mapemphero komanso miyambo yoyatsa makandulo inachitikanso malo osiyanasiyana kuphatikizapo mumzinda wa Nairobi ndipo inatsogoleredwa ndi akuluakulu a boma.
Chiwembu ngati chomwechi chinachitikanso m`dzikolo m`chaka cha 1998, pomwe gulu la Al-Qaeda linaphulitsa mabomba kumaofesi a kazembe wa dziko la America m`dzikolo ndi kupha anthu okwana 213.
Magulu a zigawenga za Al- Shabab komanso Al- Qaeda omwe kwawo ndi ku Somalia akhala akuchita ziwembu zosiyanasiyana m`dziko la Kenya posakondwa ndi kupezeka kwa asilikali a dziko la Kenya mugulu la asilikali a African Union (AU) omwe akuthandiza asilikali a dziko la Somalia kulimbana ndi zigawengazo.
Anthu m`dziko la Kenya achita mapemphero okumbukira mizimu ya anthu 148 omwe anafa pa chiwembu chomwe gulu la zigawenga za Al- Shabab zinachita pa sukulu ya ukachenjede ya Garisa m`dzikolo.
Malinga ndi malipoti awailesi ya BBC anthu mazanamazana anasokhana pa sukuluyo ndipo anachita mapemphero komanso miyambo yoyatsa makandulo inachitikanso malo osiyanasiyana kuphatikizapo mumzinda wa Nairobi ndipo inatsogoleredwa ndi akuluakulu a boma.
Chiwembu ngati chomwechi chinachitikanso m`dzikolo m`chaka cha 1998, pomwe gulu la Al-Qaeda linaphulitsa mabomba kumaofesi a kazembe wa dziko la America m`dzikolo ndi kupha anthu okwana 213.
Magulu a zigawenga za Al- Shabab komanso Al- Qaeda omwe kwawo ndi ku Somalia akhala akuchita ziwembu zosiyanasiyana m`dziko la Kenya posakondwa ndi kupezeka kwa asilikali a dziko la Kenya mugulu la asilikali a African Union (AU) omwe akuthandiza asilikali a dziko la Somalia kulimbana ndi zigawengazo.