Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Abwenzi ndi Otumikira Radio Maria mu Dayosizi ya Zomba Alonjeza Kugwilira Ntchito Limodzi

$
0
0

Ngati njira imodzi yopititsira patsogolo ntchito za Radio Maria Malawi, abwenzi a wailesiyi ku dayosizi ya Zomba ati agwira ntchito limodzi ndi  otumikira a wailesiyi  potolera thandizo.

Wapampando wa bungwe  la abwenzi a Radio Maria mu dayosiziyi a Patrick Koloko ndi omwe  anena izi ku Studio yaying`ono ya Zomba pa msonkhano wa abwenzi komanso otumikira wailesiyi omwe cholinga chake chinali kulimbikitsa ubale pakati pawo.

A Koloko ati  chaka chino kuli ntchito  zambiri zoti agwire zopezera thandizo monga Mariatona, Ulendo wa ndawala komanso ma Promotion zomwe ati zikufunika kuti maguluwa agwirile ntchito limodzi.

Iwo alonjezanso kuti abwenziwa azigula magetsi a Transmitter ya ku Zomba  ndi cholinga choti wailesiyi isamazime m`derali.

Ndipo m`mawu ake mkulu woyang`anira Studio-yi, Mai Elizabeth Mitha ati ali ndi chikhulupirilo kuti kubwera pamodzi kwa otumikirawa komanso abwenzi awailesiyi kuthandiza kupeza thandizo lochuluka pa nthawi ya Mariatona.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>