Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Papa Francisco wati Akhristu Akhale Apostoli komanso Wapempha Mtendere Mdziko la Ukraine

$
0
0

Pamene mpingo umachita chaka cha  lamulungu la chifundo, mtsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Francisco wapempha akhristu kuti akhale apostoli a chifundo kwa onse osowa.

Malipoti a wailesi ya Vatican ati Papa amalankhula izi lero pa mwambo wa nsembe ya misa pa bwalo la St Peters ku likulu la mpingowu ku Vatican.

Papa wati kukhala mpostoli wa chifundo zikutanthauza kuti akhristu akuyenera kuthandiza onse omwe akukumana ndi mavuto  osiyanasiyana powathandiza kuti asendere chifupi ndi Mulungu.

Pa mwambowu Papa wapemphanso mtendere mdziko la Ukraine poganizira mavuto omwe anthu a mdzikolo akukumana nawo.

Mtsogoleri wa mpingo wakatolikayu wati anthu ambiri  omwe akuvutika kaamba ka ziwembu zomwe zikuchitika mmaiko a ku Europe, ndi anthu okalamba komanso ana.

Iye wati kuphatikiza kuwayikiza mmapemphero anthuwa, lamulungu la pa 24 mwezi uno chopereka chonse cha mmatchalitchi a mmaiko a ku Europe chidzakhale chothandizira anthuwa.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>