Anthu asanu afa ndipo ena asanu ndi awiri avulala kamba ka bomba lomwe linaphulitsidwa pa malo ena odyera mu mzinda wa Mogadishu mdziko la Somalia.
Malinga ndi malipoti a wailesi ya BBC munthu yemwe wachita izi ati anayimitsa galimoto lake panja pa malowo momwe munali bomba lomwe linaphulitsidwalo.
Malipoti ati gulu la zigawenga za chisilamu za Al-Shabab lavomera kuti ndi lomwe lachita chiwembuchi.
Gululi lomwe lili pansi pa gulu la zigawenga za Al-Qaeda lakhala likuchita za uchifwamba mdziko la Somalia kuyambira mu chaka cha 2011.
Anthu asanu afa ndipo ena asanu ndi awiri avulala kamba ka bomba lomwe linaphulitsidwa pa malo ena odyera mu mzinda wa Mogadishu mdziko la Somalia.
Malinga ndi malipoti a wailesi ya BBC munthu yemwe wachita izi ati anayimitsa galimoto lake panja pa malowo momwe munali bomba lomwe linaphulitsidwalo.
Malipoti ati gulu la zigawenga za chisilamu za Al-Shabab lavomera kuti ndi lomwe lachita chiwembuchi.
Gululi lomwe lili pansi pa gulu la zigawenga za Al-Qaeda lakhala likuchita za uchifwamba mdziko la Somalia kuyambira mu chaka cha 2011.