Anthu khumi afa ndipo ena 62 avulala bus yomwe anakwera itachita ngozi mdera la Songo mdziko la Mozambique.
Malinga ndi malipoti bus-yo yomwe ndi ya Kampani ya Nyamende nambala yake KMZ 56 ZN imachokera mdziko la South Africa kupita mu mzinda wa Blantyre ndipo inanyamula mzika za mdziko la Malawi.
Akuluakulu a basiyo ati padakali pano anthu omwe avulalawo agonekedwa ku chipatala chachikulu cha Mwanza.