M’modzi mwa akatswiri poyimba nyimbo za uzimu m’dziko muno, PAUL BANDA wati mayimbidwe mu mpingo wakatolika, angapite patsogolo komanso kuyenda bwino, pokhapokha magulu oyimba mu mpingowu atazamitsa luso lomapeka nyimbo zawo kuchokera m’buku Loyera.
Paul Banda, wati kwanthawi, yayitali tsopano magulu oyimba mu mpingo wakatolika, akhala akungokopera mayimbidwe a magulu oyimba akunja mkumatulutsa zimbale, mchitidwe womwe wakhala ukubwezeretsa m’mbuyo luso la mayimbidwe m`magulu oimba ambiri a mpingowu m’dziko muno. Iye wayamikira kwaya zomwe zafika pa mlingo wotha kumapeka zokha nyimbo, atazindikira kuipa kongokopera luso la kwaya zina zomwe zkuchita bwino.