Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Akhristu Akhale Olimba Mtima pa Chikhristu Ngati Amalitiri a ku Uganda

$
0
0

Akhristu a mpingo wakatolika awapempha kuti atengere chitsanzo cha kulimba mtima pa chikhristu chawo monga momwe anachitira Amalitiri 22 a ku Uganda polora kuphedwa kamba chikhulupiliro chawo.

Episkopi wa dayosizi ya Kiyinda Mityana m’dzikomo ambuye Joseph Anthony Zziwandi yemwe wanena izi pa mwambo wa misa  ya chaka cha chokumbukira Amalitiri-wa omwe unachitikira ku malo oyera mu mpingowu a Namugongo omwe akupezeka mu mzinda wa Kampala m’dziko-mo .

Mwambo wa a malitiri wa chaka chino wachitika pa mutu woti Chilungamo ndi chimene chidzakumasuleni.”

Ambuye-wa ati akhristu akuyenera kuima pa choona kamba koti ndi chimene chidzawamasule komanso kutukula dziko lonse.

Ku mwambowu kunafika atsogoleri ndi akhristu a mpingowu ochokera m’maiko osiyanasiyana kuphatikizaponso a kuno ku Malawi.

 

 

 

 

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>