Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Msonkhano wa PMS Watha Lachisanu

$
0
0

M’sonkhano waukulu wa masiku anayi wa atsogoleri oyendetsa ma bungwe a utumiki wa a Papa m’ma dayosizi onse ampingo wakatolika mdziko muno watha lachisanu.

Polankhula pambuyo pa msonkhanowu omwe unachitikira mu dayosizi ya Mzuzu, mkulu wa bungwe loyendetsa mabungwe-wa mdziko muno la Pontifical Mission Societies (PMS),Bambo Vincent Mwakhwawaati ku msonkhanowu akambirana za misonkhano komanso miyambo yomwe ikuyembekezeka kuchitika kutsogoloku monga maphunziro a aphunzitsi a utumiki wa ana komanso chaka cha chibalalitso.

Iwo ati pa msonkhanowu awunikirananso momwe angagwilire ntchito ngati atsogoleri m’madayosizi awo.

Polankhulapo m’modzi mwa atsogoleri omwe anali nawo pa msonkhanowu omwenso angosankhidwa kumene pa udindowu, Bambo Paul Rappozo, ati msonkhanowu wawapindulira kamba koti mfundo zomwe akambirana ziwathandiza kutumikira bwino pa udindowu.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>